Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 23:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo iwo akuimirirako anati, Ulalatira kodi mkulu wa ansembe wa Mulungu?

5. Ndipo Paulo anati, Sindinadziwa, abale, kuti ndiye mkulu wa ansembe; pakuti kwalembedwa, Usamnenera coipa mkulu wa anthu ako.

6. Koma pozindikira Paulo kuti ena ndi Asaduki, ndi ena Afarisi, anapfuula m'bwalomo, Amuna, abale, ine ndine Mfarisi, mwana wa Afarisi: andinenera mlandu wa ciyembekezo ndi kuuka kwa akufa.

7. Ndipo pamene adatero, kunakhala cilekano pakati pa Afarisi ndi Asaduki; ndipo osonkhanawo anagawikana.

8. Pakutitu Asaduki anena kuti kulibe kuuka kwa akufa, kapena mngelo, kapena mzimu; koma Afarisi abvomereza ponse pawiri.

9. Ndipo cidauka cipolowe cacikuru; ndipo alembi ena a kwa Afarisi anaimirira, natsutsana, nanena, Sitipeza coipa ciri conse mwa munthuyu; ndipo nanga bwanji ngati mzimu kapena mngelo: walankhula naye?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 23