Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 21:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo m'mene tinapeza ngalawa Yakuoloka kunka ku Foinike, tinalowamo, ndi kupita nayo.

3. Ndipo pamene tinafika popenyana ndi Kupro, tinacisiya kulamanzere, ntinapita ku Suriya; ndipo tinakoceza ku Turo; pakuti pamenepo ngalawainafuna kutula akatundu ace.

4. Ndipo m'mene tinapeza ophunzira, tinakhalako masikuasanu ndi awiri; ndipo iwowa ananena ndi Paulo mwa Mzimu, kuti asakwere ku Yerusalemu.

5. Ndipo kunali pamene tidatsiriza masikuwa, tidacoka ndi kunka ulendo wathu; ndipo iwo onse, akazi ndi ana anatiperekeza kufikira kuturuka m'mudzi; ndipo pogwadira pa mcenga wa kunyanja, tinapemphera,

6. ndi kulawirana; ndipo tinalowa m'ngalawa, koma iwo anabwera kwao.

7. Ndipo ife titatsiriza ulendo wathu wocokera ku Turo, tinafika ku Ptolemayi; ndipo m'mene tidalankhula abale, tinakhala nao tsiku limodzi.

8. Ndipo m'mawa mwace tinacoka, ntinafika ku Kaisareya, ndipo m'mene tinalowa m'nyumba ya Filipo mlaliki, mmodzi wa asanu ndi awiri aja, tinakhala naye.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 21