Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 21:10-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo pokhalapo masiku ambiri, anatsika ku Yudeya mneneri, dzina lace Agabo.

11. Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a m'Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.

12. Koma pamene tinamva izi tinamdandaulira ife ndi iwo a komweko, asakwere iye kunka ku Yerusalemu.

13. Pamenepo Paulo anayankha, Mucitanji, polira ndi kundiswera mtima? pakuti ndakonzeka Ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu cifukwa ca dzina la Ambuye Yesu.

14. Ndipo pokana iye kukopeka, tinaleka, ndi kuti, Kufuna kwa Ambuye kucitidwe.

15. Ndipo atapita masiku awa tinakonza akatundu athu, ntikwera ku Yerusalemu.

16. Ndipo anamuka nafenso ena a ophunzira a ku Kaisareya, natenganso wina Mnaso wa ku Kupro, wophunzira wakale, amene adzaticereza.

17. Ndipo pofika ife ku Yerusalemu, abale anatilandira mokondwera.

18. Ndipo m'mawa mwace Paulo analowa nafe kwa Yakobo; ndi akulu onse anali pomwepo.

19. Ndipo atawalankhula iwo, anawafotokozera cimodzi cimodzi zimene Mulungu anacita kwa amitundu mwa utumiki wace.

20. Ndipo pamene anazimva, analemekeza Mulungu; nati kwa iye, Uona, mbale, kuti ambirimbiri mwa Ayuda akhulupira; ndipo ali naco cangu onsewa, ca pa cilamulo;

21. ndipo anamva za iwe, kuti uphunzitsa Ayuda onse a ku amitundu apatukane naye Mose, ndi kuti asadule ana ao, kapena asayende monga mwa miyambo.

22. Nciani tsono? adzamva ndithu kuti wafika.

23. Cifukwa cace ucite ici tikuuza iwe; tiri nao amuna anai amene anawinda;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 21