Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 19:27-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. ndipo tiopa ife kuti nchito yathuyi idzayamba kunyonyosoka; komanso kuti kacisi wa mlungu wamkazi Artemi adzayamba kuyesedwa wacabe; ndiponso kuti iye adzayamba kutsitsidwa ku ukulu wace, iye amene a m'Asiya onse, ndi onse a m'dziko lokhalamo anthu, ampembedza.

28. Ndipo pamene anamva, anadzala ndi mkwiyo, napfuula, nati, Wamkuru ndi Artemi wa ku Efeso,

29. Ndipo m'mudzi monse munacita piringu-piringu, nathamangira onse pamodzi ku bwalo losewera, atagwira Gayo ndi Aristarko, anthu a ku Makedoniya, alendo anzace a Paulo.

30. Ndipo pamene Paulo anafuna kulowa kwa anthu, akuphunzira ace sanamloleza.

31. Ndipo akulu ena a Asiyanso, popeza anali abwenzi ace, anatumiza mau kwa iye, nampempha asadziponye ku bwalo lakusewera.

32. Ndipo ena anapfuula kanthu kena, ena kanthu kena; pakuti msonkhanowo unasokonezeka; ndipo unyinji sunadziwa cifukwa cace ca kusonkhana.

33. Ndipo anaturutsa Alesandro m'khamumo, kumturutsa iye Ayuda. Ndipo Alesandro anatambasula dzanja, nafuna kudzikanira kwa anthu adasonkhanawo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 19