Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 18:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitapita izi anacoka ku Atene, nadza ku Korinto.

2. Ndipo anapeza Myuda wina dzina lace Akula, pfuko lace la ku Ponto, atacoka catsopano ku Italiya, pamodzi ndi mkazi wace Priskila, cifukwa Klaudiyo analamulira Ayuda onse acoke m'Roma; ndipo Pauloanadza kwa iwo:

3. ndipo popeza anali wa nchito imodzimodzi, anakhala nao, ndipo iwowa anagwira nchito; pakuti nchito yao inali yakusoka mahema.

4. Ndipo anafotokozera m'sunagogemasabata onse, nakopa Ayuda ndi Ahelene.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 18