Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 17:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma iwo amene anaperekeza Paulo anadza naye kufikira ku Atene; ndipo polandira iwo lamulo la kwa Sila ndi Timoteo kuti afulumire kudza kwa iye ndi cangu conse, anacoka.

16. Pamene Paulo analindira iwo pa Atene, anabvutidwa mtima pamene anaona mudzi wonse wadzala ndi mafano.

17. Cotero tsono anatsutsana ndi Ayuda ndi akupembedza m'sunagoge, ndi m'bwalo la malonda masiku onse ndi iwo amene anakomana nao.

18. Ndipo akukonda nzeru ena a Epikureya ndi a Stoiki anatengana naye. Ena anati, ici ciani afuna kunena wobwetuka uyu? Ndipo ena, Anga wolalikira ziwanda zacilendo, cifukwa analalikira Yesu ndi kuuka kwa akufa.

19. Ndipo anamgwira, nanka naye ku Areopagi, nati, Kodi tingathe kudziwa ciphunzitso ici catsopano ucinena iwe?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 17