Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 16:4-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pamene anapita kupyola pamidzi, anapereka kwa iwo malamulo awasunge, amene analamulira atumwi ndi akuru a pa Yerusalemu.

5. Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku ndi tsiku.

6. Ndipo anapita pa dziko la Frugiya ndi Galatiya, atawaletsa Mzimu Woyera kuti asalalikire mau m'Asiya; pamene anafika kundunji kwa Musiya,

7. anayesa kunka ku Bituniya; ndipo Mzimu wa Yesu sanawaloleza;

8. ndipo pamene anapita pambali pa Musiya, anatsikira ku Trowa.

9. Ndipo masomphenya anaonekera kwa Paulo usiku: Panali munthu wa ku Makedoniya alinkuimirira, namdandaulira kuti, Muolokere ku Makedoniya kuno, mudzatithangate ife.

10. Pamene anaona masomphenyawo, pomwepo tinayesa kuturukirakunka ku Makedoniya, poganizira kuti Mulungu anaitanira ife kulalikira Uthenga Wabwino kwa iwo.

11. Cotero tinacokera ku Trowa m'ngalawa, m'mene tinalunjikitsa ku Samotrake, ndipo m'mawa mwace ku Neapoli;

12. pocokera kumeneko tinafika ku Filipi, mudzi wa ku Makedoniya, waukuru wa m'dzikomo, wa miraga ya Roma; ndipojidagona momwemo masiku ena.

13. Tsiku la Sabata tinaturuka kumudzi kunka ku mbali ya mtsinje, kumene tinaganizira kuti amapempherako; ndipo tinakhala pansi ndi kulankhula ndi akazi amene adasonkhana,

14. Ndipo anatimva mkazi wina dzina lace Lidiya, wakugulitsa cibakuwa, wa ku mudzi wa Tiyatira, amene anapembedza Mulungu; mtima wace Ambuye anatsegula, kuti amvere zimene anazinena Paulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 16