Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 10:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo pokayika-kayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti ciani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Komeliyo, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pa cipata,

18. ndipo anaitana nafunsa ngati Simoni, wochedwanso Petro, acerezedwako.

19. Ndipo m'mene Petro analingirira za masomphenya, Mzimu ananena naye, Taona, amuna atatu akufuna iwe.

20. Komatu tauka, nutsike, ndipo upite nao, wosakayika-kayika; pakuti ndawatuma ndine.

21. Ndipo Petro anatsikira kwa anthuwo, nati, Taonani, ine ndine amene mumfuna; cifukwa cace mwadzera nciani?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 10