Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:37-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo panali, m'mawa mwace, atatsika m'phiri, khamu lalikuru la anthu linakomana naye.

38. Ndipo onani, anapfuula munthu wa m'khamulo, nanena, nati, Mphunzitsi, ndikupemphani, yang'anirani mwana wanga; cifukwa ndiye mmodzi yekha wa ine:

39. ndipo onani, umamgwira iye mzimu, napfuula modzidzimuka; ndipo umamng'amba iye ndi kumcititsa thobvu pakamwa, nucoka pa iye mwa unyenzi, numgola iye.

40. Ndipo ndinapempha ophunzira anu kuti auturutse; koma sanathe.

41. Ndipo Yesu anayankha, nati, Ha! obadwa inu osakhulupirira ndi amphulupulu, ndidzakhala ndi inu nthawi yanji, ndi kulekerera inu? idza naye kuno mwana wako.

42. Ndipo akadadza iye, ciwandaco cinamgwetsa, ndi kumng'ambitsa, Koma Yesu anadzudzula mzimu wonyansawo, naciritsa mnyamata, nambwezera iye kwa atate wace.

43. Ndipo onse anadabwa pa ukulu wace wa Mulungu.Koma pamene onse analikuzizwa ndi zonse anazicita, iye anati kwa ophunzira ace,

44. Alowe mau ame: newa m'makutu anu; pakuti Mwana wa munthu adzaperekedwa m'manja a anthu.

45. Koma iwo sanadziwitse mau awa, ndipo anabisidwa kwa iwo, kuti asawadziwe; ndipo anaopa kumfunsa za mau awa.

46. Ndipo anayamba kutsutsana kuti wamkulu mwa iwo ndani.

47. Koma Yesu pakuona kutsutsana kwa mitima yao, anatenga kamwana, nakaimika pambali pace, nati kwa iwo,

48. Amene ali yense akalandire kamwana aka m'dzina langa alandira Ine; ndipo amene andilandira Ine alandira iye amene anandituma Ine; pakuti iye wakukhala wamng'onong'ono wa inu nonse, yemweyu ndiye wamkuru.

49. Ndipo Yohane anayankha nati, Ambuye, tinaona wina alikuturutsa ziwanda m'dzina lanu; ndipo tinamletsa, cifukwa satsatana nafe.

50. Koma Yesu anati kwa iye, Musamletse, pakuti iye amene satsutsana nanu athandizana nanu.

51. Ndipo panali, pamene anayamba kukwanira masiku akuti alandiridwe iye kumwamba, Yesu anatsimika kuloza nkhope yace kunka ku Yerusalemu,

Werengani mutu wathunthu Luka 9