Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:31-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. amene anaonekera m'ulemerero, nanenaza kumuka kwace kumene iye ati adzatsiriza ku Yerusalemu.

32. Koma Petro ndi iwo anali naye analemedwa ndi tulo; koma m'mene anayera m'maso ndithu, anaona ulemerero wace, ndi amuna awiriwo akuimirira ndi iye.

33. Ndipo panali polekana iwo aja ndi iye, Petro anati kwa Yesu, Ambuye, nkwabwino kuti tiri pano; ndipo timange misasa itatu, umodzi wa Inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya; wosadziwa iye cimene alikunena.

34. Ndipo akadalankhula izi, unadza mtambo, nuwaphimba iwo; ndipo anaopa pakulowa iwo mumtambo.

35. Ndipo munaturuka mau mumtambo nanena, Uyu ndiye Mwana wanga, wosankhidwayo; mverani iye.

36. Ndipo pakutero mauwo, Yesu anapezedwa ali yekha. Ndipo iwo anakhala cete, ndipo sanauza munthu ali yense masiku aja kanthu konse ka izo anaziona.

37. Ndipo panali, m'mawa mwace, atatsika m'phiri, khamu lalikuru la anthu linakomana naye.

38. Ndipo onani, anapfuula munthu wa m'khamulo, nanena, nati, Mphunzitsi, ndikupemphani, yang'anirani mwana wanga; cifukwa ndiye mmodzi yekha wa ine:

39. ndipo onani, umamgwira iye mzimu, napfuula modzidzimuka; ndipo umamng'amba iye ndi kumcititsa thobvu pakamwa, nucoka pa iye mwa unyenzi, numgola iye.

40. Ndipo ndinapempha ophunzira anu kuti auturutse; koma sanathe.

Werengani mutu wathunthu Luka 9