Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 8:36-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndipo amene anaona anawauza iwo maciritsidwe ace a wogwidwa ciwandayo.

37. Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa Ioyandikira anamfunsa iye acoke kwa iwo; cifukwa anagwidwa ndi mantha akuru. Ndipo iye analowa m'ngalawa, nabwerera.

38. Ndipo munthuyo amene ziwanda zinaturuka mwa iye anampempha iye akhale ndi iye; koma anamuuza apite, nanena,

39. Pita kunyumba kwako, nufotokozere zazikuruzo anakucitira iwe Mulungu. Ndipo iye anacoka, nalalikira ku mudzi wonse zazikuruzo Yesu anamcitira iye,

40. Ndipo pakubwera Yesu, khamu la anthu linamlandira iye; pakuti onse analikumlindira iye.

41. Ndipo onani, panadza munthu dzina lace Yairo, ndipo iye ndiye mkuru wa sunagoge; ndipo anagwa pamapazi ace a Yesu, nampempha iye adze kunyumba kwace;

42. cifukwa anali naye mwana wamkazi mmodzi yekha, wa zaka zace ngati khumi ndi ziwiri, ndipo analinkumwalira iye, Koma pakupita iye anthu a mipingo anakanikizana naye,

43. Ndipo mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, amene adasudzula asing'anga za moyo wace zonse, ndipo sanathe kuciritsidwa ndi mmodzi yense,

44. anadza pambuyo pace, nakhudza mphonje yacobvala cace; ndipo pomwepo nthenda yace inaleka.

Werengani mutu wathunthu Luka 8