Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:23-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo wodala iye amene sakhomudwa cifukwa ca Ine.

24. Ndipo atacoka amithenga ace a Yohane, iye anayamba kunena za Yohane kwa anthu a makamu aja, nati, Munaturuka kunka kucipululu kukapenya ciani? Bango logwedezeka ndi mphepo kodi?

25. Koma munaturuka kukaona ciani? Munthu wobvala zobvala zofewa kodi? Onani, iwo akubvala zolemera, ndi akukhala odyerera, ali m'makuka a mafumu.

26. Koma munaturuka kukaona ciani? Mneneri kodi? Etu, ndinena kwa inu, ndipo wakuposa mneneri.

27. Uyu ndi iye amene kunalembedwa za iye,Ona, ndituma Ine mthenga wanga akutsogolere,Amene adzakukonzera njira yako pamaso pako.

28. Ndinena kwa inu, kuti, Mwa akubadwa ndi akazi palibe mmodzi wamkuru woposa Yohane; koma iye amene ali wamng'ono mu Ufumu wa Mulungu amposa iye.

29. Ndipo anthu onse ndi amisonkho omwe, pakumva, anabvomereza kuti Mulungu ali wolungama, popeza anabatizidwa iwo ndi ubatizo wa Yohane.

30. Koma Afarisi ndi acilamulo anakaniza uphungu wa Mulungu kwa iwo okha, popeza sanabatizidwa ndi iye.

Werengani mutu wathunthu Luka 7