Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Nthawi yomweyo iye anaciritsa anthu ambiri nthenda zao, ndi zobvuta, ndi mizimu yoipa; napenyetsanso anthu akhungu ambiri.

22. Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Mukani, muuze Yohane zimene mwaziona, nimwazimva; anthu akhungu alandira kuona kwao, opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ogontha akumva, akufa aukitsidwa, kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.

23. Ndipo wodala iye amene sakhomudwa cifukwa ca Ine.

24. Ndipo atacoka amithenga ace a Yohane, iye anayamba kunena za Yohane kwa anthu a makamu aja, nati, Munaturuka kunka kucipululu kukapenya ciani? Bango logwedezeka ndi mphepo kodi?

25. Koma munaturuka kukaona ciani? Munthu wobvala zobvala zofewa kodi? Onani, iwo akubvala zolemera, ndi akukhala odyerera, ali m'makuka a mafumu.

Werengani mutu wathunthu Luka 7