Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Yesu adamariza mau ace onse m'makutu a anthu, analowa m'Kapernao.

2. Ndipo kapolo wa kenturiyo, wokondedwa naye, anadwala, nafuna kutsirizika.

3. Ndipo pamene iye ana-I mva za Yesu, anatuma kwa iye akuru a Ayuda, namfunsa iye kuti adze kupulumutsa kapolo wace.

4. Ndipo iwo, pakufika kwa Yesu, anampempha iye koumirira, nati, Ayenera iye kuti mumcitire ici;

5. pakuti akonda mtundu wathu, ndipo anatimangira ife sunagoge.

6. Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika iye tsono pafupi panyumba yace, kenturiyo anatuma kwa iye abwenzi ace, kunena naye, Ambuye, musadzibvute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa chindwi langa;

7. cifukwa cace ine sindinadziyesera ndekha woyenera kudza kwa Inu: koma nenani mau, ndipo mnyamata wanga adzaciritsidwa.

8. Pakuti inenso ndiri munthu wakumvera akuru anga, ndiri nao asilikari akumvera ine: ndipo ndinena kwa uyu, Muka, namuka; ndi kwa wina, Idza, nadza; ndipo kwa kapolo wanga Tacita ici, nacita.

9. Koma Yesu pakumva zimenezo anazizwa naye, napotolokera kwa anthu a mpingo wakumtsata iye, nati, Ndinena kwa inu, sindinapeza, ngakhale mwa Israyeli, cikhulupiriro cacikuru cotere.

10. Ndipo pakubwera ku nyumba otumidwawo, anapeza kapoloyo wacira ndithu.

11. Ndipo kunali, katapita kamphindi, iye ana pita kumudzi, dzina lace Nayini; ndipo ophunzira ace ndi mpingo waukuru wa anthu anapita nave.

Werengani mutu wathunthu Luka 7