Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 5:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali nayo mphamvu pa dziko lapansi yakukhululukira macimo, (anati iye kwa wamanjenjeyo), Ndinena kwa iwe, Tauka, nusenze kama wako, numuke kunyumba kwako.

25. Ndipo pomwepo anaimirira pamaso pao, nasenza cimene adagonapo, nacokapo, kunka kunyumba kwace, wakulemekeza Mulungu.

26. Ndipo cizizwo cinagwira anthu onse, ndipo analemekeza Mulungu nadzazidwa ndi mantha, nanena kuti, Lero taona zodabwitsa.

27. Ndipo zitatha izi iye anaturuka, Danna munthu wamsonkho, dzina lace Levi, alikukhala polandira msonkho, nati kwa iye, Unditsate Ine.

28. Ndipo iye anasiya zonse, nanyamuka, namtsata iye.

Werengani mutu wathunthu Luka 5