Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 5:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo iye, pakuona cikhulupiriro cao, anati, Munthu iwe, macimo ako akhululukidwa.

21. Ndipo alembi ndi Afarisi anayamba kuyesayesa mumtima mwao, kuti, ndani Uyu alankhula zomcitira Mulungu mwano? Ndani angathe kukhululukira macimo, koma Mulungu yekha?

22. Koma Yesu anadziwa zoyesayesa zao, nayankha, nati kwa iwo, Muyesayesa bwanji m'mitima yanu?

23. Capafupi nciti, kunena, Akhululukidwa kwa iwe macimo ako; kapena kunena, Tauka, nuyende?

24. Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali nayo mphamvu pa dziko lapansi yakukhululukira macimo, (anati iye kwa wamanjenjeyo), Ndinena kwa iwe, Tauka, nusenze kama wako, numuke kunyumba kwako.

25. Ndipo pomwepo anaimirira pamaso pao, nasenza cimene adagonapo, nacokapo, kunka kunyumba kwace, wakulemekeza Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Luka 5