Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:30-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Koma iye anapyola pakati pao, nacokapo.

31. Ndipo iye anatsika nadza ku Kapernao, ndiwo mudzi wa ku Galileya, Ndipo analikuwaphunzitsa iwo pa Sabata; ndipo anadabwa ndi ciphunzitso cace;

32. cifukwa mau ace anali ndi ulamuliro.

33. Ndipo munali m'sunagoge munthu, wokhala naco ciwanda conyansa; napfuula ndi mau olimba, kuti,

34. Ha! tiri ndi ciani ndi Inu, Yesu wa ku N azarete? kodi munadza kutiononga ife? ndikudziwani Inu muli yani, ndinu Woyera wace wa Mulungu.

35. Ndipo Yesu anamdzudzula iye, nanena, Tonthola, nuturuke mwa iye. Ndipo ciwandaco m'mene cinamgwetsa iye pakati, cinaturuka mwa iye cosampweteka konse.

36. Ndipo anthu onse anadabwa, nalankhulana wina ndi mnzace, nanena, Mau amenewa ali otani? cifukwa ndi ulamuliro ndi mphamvu angolamulira mizimu yonyansa, ndipo ingoturuka.

37. Ndipo mbiri yace ya iye inafalikira ku malo onse a dziko Ioyandikira.

Werengani mutu wathunthu Luka 4