Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Kulalikira caka cosankhika ca Ambuye.

20. Ndipo m'mene iye anapinda bukulo, nalipereka kwa mnyamata, anakhala pansi; ndipo maso ao a anthu onse m'sunagogemo anamyang'anitsa iye.

21. Ndipo anayamba kunena kwa iwo, kuti, Lero lembo ili lakwanitsidwa m'makutu anu.

22. Ndipo onse anamcitira iye umboni nazizwa ndi mau a cisomo akuturuka m'kamwa mwace; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?

23. Ndipo anati kwa iwo, Kwenikweni mudzati kwa Ine nkhani iyi, Sing'anga iwe, tadziciritsa wekha: zonse zija tazimva zinacitidwa ku Kapernao, muzicitenso zomwezo kwanu kuno.

24. Ndipo iye anati, Indetu, ndinena kwa inu, kuti, Palibe mneneri alandirika ku dziko la kwao.

25. Koma zoonadi ndinena kwa inu, kuti, Munali akazi amasiye ambiri m'lsrayeli masiku ace a Eliya, pamene kunatsekedwa kumwamba zaka zitatu ndi miyezi isanu ndi umodzi, pamene panakhala njala yaikuru pa dziko lonselo;

Werengani mutu wathunthu Luka 4