Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:39-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo mmodzi wa ocita zoipa anapacikidwawo anamcitira iye mwano nanena, Kodi suli Kristu Iwe? udzipulumutse wekha ndi ife.

40. Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m'kulangika komweku?

41. Ndipo ifetu kuyenera; pakuti tirikulandira zoyenera zimene tinazicita: koma munthu uyu sanacita kanthu kolakwa.

42. Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukileni m'mene mulowa Ufumuwanu.

43. Ndipo Iye ananena naye, Indetu, ndinena ndi iwe, Lero lino udzakhala ndine m'Paradaiso.

44. Ndipo ora lace pamenepo linali ngati lacisanu ndi cimodzi. Ndipo panali mdima pa dziko lonse kufikira ora lacisanu ndi cinai, ndipo dzuwa linada.

45. Ndipo nsaru yocinga ya m'Kacisi inang'ambika pakati.

46. Ndipo pamene Yesu anapfuula ndi mau akuru, anati, 1 Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wace.

Werengani mutu wathunthu Luka 23