Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:38-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Ndipo kunalinso lembo pamwamba pace, ndilo: UYU NDIYE MFUMU YAAYUDA.

39. Ndipo mmodzi wa ocita zoipa anapacikidwawo anamcitira iye mwano nanena, Kodi suli Kristu Iwe? udzipulumutse wekha ndi ife.

40. Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m'kulangika komweku?

41. Ndipo ifetu kuyenera; pakuti tirikulandira zoyenera zimene tinazicita: koma munthu uyu sanacita kanthu kolakwa.

42. Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukileni m'mene mulowa Ufumuwanu.

43. Ndipo Iye ananena naye, Indetu, ndinena ndi iwe, Lero lino udzakhala ndine m'Paradaiso.

44. Ndipo ora lace pamenepo linali ngati lacisanu ndi cimodzi. Ndipo panali mdima pa dziko lonse kufikira ora lacisanu ndi cinai, ndipo dzuwa linada.

Werengani mutu wathunthu Luka 23