Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 18:22-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Koma m'mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa cinthu cimodzi: gulitsa ziri zonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala naco cuma ceni ceni m'Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

23. Koma pakumva izi anagwidwa naco cisoni cambiri; pakuti anali mwini cuma cambiri.

24. Ndipo Yesu pomuona iye anati, Ha! nkubvutika nanga kwa anthu eni cuma kulowa Ufumu wa Mulungu!

25. Pakuti nkwapafupi kwa ngamila apyole diso la singano koma kwa munthu mwini cuma, kulowa Ufumu wa Mulungu nkwapatali.

26. Koma akumvawo anati, Tsono ndani angathe kupulumutsidwa?

27. Koma iye anati, Zinthu zosatheka ndi anthu zitheka ndi Mulungu.

28. Ndipo Petro anati, Taonani ife tasiya zathu za ife eni, ndipo takutsatani Inu.

29. Koma anati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Palibe munthu wasiya nyumba, kapena mkazi, kapena abale, kapena akumbala, kapena ana, cifukwa ca Ufumu wa Mulungu,

30. koma adzalandira zobwezedwa koposatu m'nthawi yino; ndipo m'nthawi irinkudza moyo wosatha.

31. Ndipo anadzitengera khumi ndi awiriwo, nati kwa iwo, Taonani, tikwera kunkaku Yerusalemu, ndipo zidzakwaniritsidwa kwa Mwana wa munthu zonse zolembedwa ndi aneneri.

32. Pakuti adzampereka kwa amitundu, nadzamseka, nadzamcitira cipongwe, nadzamthira malobvu; ndipo atamkwapula adzamupha iye;

33. ndipo tsiku lacitatu adzauka.

34. Ndipo sanadziwitsa kanthu ka izi; ndi mau awa adawabisikira, ndipo sanazindikira zonenedwazo.

Werengani mutu wathunthu Luka 18