Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:8-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pamene pali ponse waitanidwa iwe ndi munthu ku cakudya ca ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,

9. ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

10. Koma pamene pali ponse waitanidwa iwe, pita nukhale pansi pa malo a kuthungo; kotero kuti pamene akadza iye anakuitana iwe, akanena ndi iwe, Bwenzi langa, sendera, kwera kuno; pomwepo udzakhala ndi ulemerero pamaso pa onse akuseama pacakudya pamodzi ndi iwe.

11. Cifukwa munthu ali yense wakudzikuza adzacepetsedwa; ndipo wakudzicepetsa adzakulitsidwa.

12. Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza cakudya ca pausana kapena ca madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a pfuko lako, kapena anansi ako eni cuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.

13. Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;

14. ndipo udzakhala wodala; cifukwa iwo alibe cakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa oiungama.

15. Ndipo pamene wina wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye anamva izi, anati kwa iye, Wodala iye amene adzadya mkate mu Ufumu wa Mulungu.

16. Koma anati kwa iye, Munthu wina anakonza phwando lalikuru; naitana anthu ambiri;

17. ndipo anatumiza kapolo wace pa nthawi ya phwando kukanena kwa oitanidwawo, idzani, cifukwa zonse zakonzeka tsopano.

18. Ndipo onse ndi mtima umodzi anayamba kuwiringula. Woyamba anati kwa iye, Ine ndagula munda, ndipo ndiyenera ndituruke kukauona; ndikupempha undilole ine ndisafika.

19. Ndipo anati wina, Ine ndagula ng'ombe za magori asanu, ndipo ndinka kukaziyesa; ndikupempha undilole ine ndisafika.

20. Ndipo anati wina, Ine ndakwatira mkazi, ndipo cifukwa cace sindingathe kudza.

21. Ndipo kapoloyo pakubwera anauza mbuye wace zinthu izi. Pamenepo mwini nyumba anakwiya, nati kwa kapolo wace, Turuka msanga, pita kumakwalala ndi ku njira za mudzi, nubwere nao muno aumphawi ndi opunduka ndi akhungu ndi otsimphina.

22. Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, cimene munacilamulira cacitika, ndipo malo atsalapo.

23. Ndipo mbuye ananena kwa kapoloyo, Turuka, nupite kumiseu ndi njira za kuminda, nuwaumirize anthu alowe, kuti nyumba yanga idzale.

24. Pakuti ndinena kwa inu, kuti kulibe mmodzi wa amuna oitanidwa aja adzalawa phwando langa.

25. Ndipo mipingo yambiri ya anthu inamuka naye; ndipo iye anapotoloka, nati kwa iwo.

26. Munthu akadza kwa Ine, wosada atate wace ndi amace, ndi mkazi wace, ndi ana, ndi abale, ndi alongo ace, inde ndi moyo wace womwe wa iye mwini, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

27. Ndipo amene ali yense sasenza mtanda wace wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sakhoza kukhala wophunzira wanga,

Werengani mutu wathunthu Luka 14