Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:3-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Yesu anayankha nati kwa acilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuciritsa, kapena iai?

4. Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

6. Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.

7. Ndipo iye ananena fanizo kwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,

8. Pamene pali ponse waitanidwa iwe ndi munthu ku cakudya ca ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,

9. ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

10. Koma pamene pali ponse waitanidwa iwe, pita nukhale pansi pa malo a kuthungo; kotero kuti pamene akadza iye anakuitana iwe, akanena ndi iwe, Bwenzi langa, sendera, kwera kuno; pomwepo udzakhala ndi ulemerero pamaso pa onse akuseama pacakudya pamodzi ndi iwe.

11. Cifukwa munthu ali yense wakudzikuza adzacepetsedwa; ndipo wakudzicepetsa adzakulitsidwa.

12. Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza cakudya ca pausana kapena ca madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a pfuko lako, kapena anansi ako eni cuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.

13. Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;

14. ndipo udzakhala wodala; cifukwa iwo alibe cakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa oiungama.

15. Ndipo pamene wina wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye anamva izi, anati kwa iye, Wodala iye amene adzadya mkate mu Ufumu wa Mulungu.

16. Koma anati kwa iye, Munthu wina anakonza phwando lalikuru; naitana anthu ambiri;

Werengani mutu wathunthu Luka 14