Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndiponso anati, Ndidzafanizira Ufumu wa Mulungu ndi ciani?

21. Ufanana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazianatenga, nacibisa mu miyeso itatu ya ufa, kufikira unatupa wonsewo,

22. Ndipo Iye anapita pakati pa mizinda ndi midzi, naphunzitsa, nayenda ulendo kunkabe ku Yerusalemu.

23. Ndipo munthu anati kwa iye, Ambuye, akupulumutsidwandiwo owerengeka kodi? Koma iye anati kwa iwo,

24. Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza; cifukwa anthu ambiri, ndikuuzani, adzafunafuna kulowamo, koma sadzakhoza.

25. Pamene atauka mwini nyumba natseka pakhomo, ndipo inu mudzayamba kuima pabwalo, ndi kugogoda pacitseko, ndi kunena, Ambuye titsegulireni ife; ndipo iye adzayankha nadzati ndi inu, Sindidziwa inu kumene mucokerako;

26. pomwepo mudzayambakunena, Ifetinadya ndi kumwa pamaso panu, ndipo munaphunzitsa m'makwalala a kwathu;

Werengani mutu wathunthu Luka 13