Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 12:51-59 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Kodi muyesa kuti ndinadzera kudzapatsa mtendere pa dziko lapani? Ndinena wa inu, Iaitu, komatu kutsutsana;

52. pakuti 6 kuyambira tsopano adzakhala m'nyumba imodzi anthu asanu, atatu adzatsutsana ndi awiri, ndi awiri adzatsutsana ndi atatu.

53. Adzatsutsana atate ndi mwana wace, ndi mwana ndi atate wace; amace adzatsutsana ndi mwana wamkazi'l ndi mwana wamkazi ndi amace, mpongozi adzatsutsana ndi mkazi wa mwana wace, ndi mkaziyo ndi mpongozi wace.

54. Koma iye ananenanso kwa makamu a anthu, 7 Pamene pali ponse muona mtambo wokwera kumadzulo, pomwepo munena, kuti, Ikudza mvula; ndipo itero.

55. Ndipo pamene mphepo ya kumwela iomba, munena, kuti, Kudzakhala kutenthatu; ndipo kuterodi.

56. Onyenga inu, mudziwa kuzindikira nkhope yace ya dziko lapansi ndi ya thambo; koma simudziwa bwanji kuzindikira nyengoyino?

57. Ndipo inunso, pa nokha mulekeranji kuweruza kolungama?

58. Pakuti 8 pamene ulikupita naye mnzako wa miandu kwa woweruza, fulumira panjira kutha naye mlandu, kuti angakokere iwe kwa woweruza, ndipo woweruzayo angapereke iwe kwa msilikari, ndi msilikari angaponye iwe m'nyumba yandende.

59. Ine ndinena kwa iwe, 9 Sudzaturukamo konse kufikira utalipira kakobiri kakumariza.

Werengani mutu wathunthu Luka 12