Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Iye wosabvomerezana ndi Ine atsutsana ndi Ine; ndipo iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwaza.

24. Pamene pali ponse mzimu wonyansa ukaturuka mwa munthu, upyola malo opanda madzi nufunafuna mpumulo; ndipo posaupeza unena, Ndidzabwera kunyumba kwanga kumene ndinaturukako;

25. ndipo pofika, uipeza yosesa ndi yokonzeka.

26. Pomwepo, upita nutenga mizimu yina isanu ndi iwiri yoipa yoposa ndi uwu mwini; ndipo ilowa nikhalira komweko; ndipo makhalidwe otsiriza a munthu uyu aipa koposa oyambawo.

27. Ndipo kunali, pakunena izi iye, mkazi wina mwa khamu la anthu anakweza mau, nati kwa iye, Yodala mimba imene idakubalani, ndi mawere amene munayamwa.

28. Koma iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.

Werengani mutu wathunthu Luka 11