Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitatha izi Ambuye anaika ena makumi asanu ndi awiri, nawatuma iwo awiri awiri pamaso pace ku mudzi uli wonse, ndi malo ali onse kumene ati afikeko mwini.

2. Ndipo ananena kwa iwo, Dzinthu dzicuruka, koma anchito acepa; potero pemphani Mwini dzinthu, kuti akankhe anchito kukututa kwace.

3. Mukani; taonani, Ine ndituma inu ngati ana a nkhosa pakati pa mimbulu.

4. Musanyamule thumba la ndalama kapena thumba la kamba, kapena nsapato; nimusalankhule munthu panjira.

5. Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowamo muthange mwanena, Mtendere ukhale pa nyumba iyi.

Werengani mutu wathunthu Luka 10