Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 22:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anandionetsa mtsinje wa madzi a moyo, wonyezimira ngati krustalo, oturuka ku mpando wacifumu wa Mulungu ndi wa Mwanawarikhosa.

2. Pakati pa khwalala lace, ndi tsidya ili la mtsinje, ndi tsidya lace lija panali mtengo wa moyo wakubala zipatso khumi ndi ziwiri, ndi kupatsa zipatso zace mwezi ndi mwezi; ndipo masamba a mtengo ndiwo akuciritsa nao amitundu.

3. Ndipo sipadzakhalanso temberero liri lonse; ndipo mpando wacifumu wa Mulungu ndi wa Mwanawankhosa udzakhala momwemo; ndipo akapolo ace adzamtumikira iye,

4. nadzaona nkhope yace; ndipo dzina lace lidzakhala pamphumipao.

5. Ndipo sikudzakhalanso usiku; ndipo sasowa kuunika kwa nyali, ndi kuunika kwa dzuwa; cifukwa Ambuye Mulungu adzawaunikira; ndipo adzacita ufumu ku nthawi za nthawi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 22