8. Ndipo tilekerenji kunena, Ticite zoipa kuti zabwino zikadze (monganso ena atinamiza ndi kuti timanena)? Kulanga kwa amenewo kuli kolungama.
9. Ndipo ciani tsono? kodi tiposa ife? Iai ndithu; pakuti tidawaneneza kale Ayuda ndi Ahelene omwe, kuti onsewa agwidwa ndi ucimo;
10. monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;
11. Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;
12. Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.
13. M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;
14. M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;