Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 3:5-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma ngati cosalungama cathu citsimikiza cilungamo ca Mulungu, tidzatani ife? Kodi ali wosalungama Mulungu, amene afikitsa mkwiyo? (ndilankhula umo anenera munthu).

6. Msatero ai. Ngati kotero, Mulungu adzaweruza bwanji mlandu wa dziko lapansi?

7. Pakuti ngati coonadi ca Mulungu cicurukitsa ulemerero wacecifukwa ca bodza langa, nanga inenso ndiweruzidwa bwanji monga wocimwa?

8. Ndipo tilekerenji kunena, Ticite zoipa kuti zabwino zikadze (monganso ena atinamiza ndi kuti timanena)? Kulanga kwa amenewo kuli kolungama.

9. Ndipo ciani tsono? kodi tiposa ife? Iai ndithu; pakuti tidawaneneza kale Ayuda ndi Ahelene omwe, kuti onsewa agwidwa ndi ucimo;

10. monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;

11. Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;

12. Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.

13. M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;

14. M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;

15. Miyendo yao icita liwiro kukhetsa mwazi;

Werengani mutu wathunthu Aroma 3