16. Koma sanamvera Uthenga Wabwino onsewo. Pakuti Yesaya anena, Ambuye, anakhulupirira ndani zonena ife?
17. Comweco cikhulupiriro cidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Kristu.
18. Koma ine nditi, Sanamva iwo kodi! Indetu,Liu lao linaturukira ku dziko lonse lapansi,Ndi maneno ao ku malekezero a dziko lokhalamo anthu.
19. Koma nditi, Kodi Israyeli alibe kudziwa? Poyamba Mose anena,Ine ndidzacititsa inu nsanje ndi iwo amene sakhala mtundu wa anthu,Ndidzakwiyitsa inu ndi mtundu wopulukira.