Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 2:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti ngati mau adalankhulidwa ndi angelo adakhala okhazikika, ndipo colakwira ciri conse ndi cosamvera calandira mphotho yobwezera yolungama,

3. tidzapulumuka bwanji ife, tikapanda kusamala cipulumutso cacikuru cotero? cimene Ambuye adayamba kucilankhula, ndipo iwo adacimva anatilimbikitsira ife;

4. pocita umboni pamodzi nao Mulungunso ndi zizindikilo, ndi zozizwitsa ndi mphamvu za mitundu mitundu ndi zogawira za Mzimu Woyera, monga mwa cifuniro cace.

5. Pakuti sanagoniersera angelo dziko lirinkudza limene tinenali.

6. Koma wina anacita umboni pena, nati,Munthu nciani kuti mumkumbukila iye?Kapena mwana wa munthu kuti muceza naye?

7. Munamcepsa pang'ono ndi angelo,Mudambveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu,Ndipo mudamuika iye wovang'anira nchito za manja anu;

Werengani mutu wathunthu Ahebri 2