Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 2:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwa ici tiyenera kusamaliradi zimene tidazimvazi kuti kapena tingatengedwe ndi kusiyana nazo.

2. Pakuti ngati mau adalankhulidwa ndi angelo adakhala okhazikika, ndipo colakwira ciri conse ndi cosamvera calandira mphotho yobwezera yolungama,

3. tidzapulumuka bwanji ife, tikapanda kusamala cipulumutso cacikuru cotero? cimene Ambuye adayamba kucilankhula, ndipo iwo adacimva anatilimbikitsira ife;

4. pocita umboni pamodzi nao Mulungunso ndi zizindikilo, ndi zozizwitsa ndi mphamvu za mitundu mitundu ndi zogawira za Mzimu Woyera, monga mwa cifuniro cace.

5. Pakuti sanagoniersera angelo dziko lirinkudza limene tinenali.

6. Koma wina anacita umboni pena, nati,Munthu nciani kuti mumkumbukila iye?Kapena mwana wa munthu kuti muceza naye?

Werengani mutu wathunthu Ahebri 2