Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 12:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. amene mau ace anagwedeza dziko pamenepo; koma tsopano adalonjeza, ndi kuti, Kamodzinso ndidzagwedeza, si dziko lokha, komanso m'mwamba.

27. Ndipo ici, cakuti kamodzinso, cilozera kusuntha kwace kwa zinthu zogwedezeka, monga kwa zinthu zolengedwa, kuti zinthu zosagwedezeka zikhale.

28. Mwa ici polandira ufumu wosagwedezeka, tikhale naco cisomo, cimene tikatumikire naco Mulungu momkondweretsa, ndi kumcitira ulemu ndi mantha.

29. Pakuti 1 Mulungu wathu ndiye mota wonyeketsa.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 12