Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. KALE Mulungu analankhula ndi makolo mwa aneneri m'manenedwe ambiri ndi mosiyana-siyana,

2. koma pakutha pace pa masiku ano analankhula ndi ife ndi Mwana amene anamuika wolowa nyumba wa zonse, mwa Iyenso analenga maiko ndi am'mwamba omwe;

3. ameneyo, pokhala ali cinyezimiro ca ulemerero wace, ndi cizindikilo ceni ceni ca cikhalidwe cace, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yace, m'mene adacita ciyeretso ca zoipa, anakhala pa dzanja lamanja la Ukulu m'Mwamba,

4. atakhala wakuposa angelo, monga momwe adalowa dzina lakuposa iwo.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 1