Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 6:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Koma tisaleme pakucita zabwino pakuti pa nyengo yace tidzatuta tikapanda kufoka.

10. Cifukwa cace, monga tiri nayo nyengo, ticitire onse cokoma, koma makamaka iwo a pa banja la cikhulupiriro.

11. Taonani, malembedwe akuruwo ndakulemberani inu ndi dzanja langa la ine mwini.

12. Onseamene afuna kuonekera okoma m'thupi, iwowa akukangamizani inu mudulidwe; cokhaco, cakuti angazunzike cifukwa ca mtanda wa Kristu.

13. Pakuti angakhale iwo omwe odulidwa sasunga lamulo; komatu afuna inu mudulidwe, kuti akadzitamandire m'thupi lanu.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 6