Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 6:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse cilamulo ca Kristu.

3. Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali cabe, adzinyenga yekha.

4. Koma yense ayesere nchito yace ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira cifukwa ca iye yekha, si cifukwa ca wina,

5. Pakuti yense adzasenza katundu wace wa iye mwini.

6. Koma iye amene aphunzira mau, ayenera kucereza womphunzitsayo m'zonse zabwino.

7. Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti cimene munthu acifesa, cimenenso adzacituta.

8. Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, cocokera m'thupi adzatuta cibvundi; koma wakufesera kwa Mzimu, cocokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

9. Koma tisaleme pakucita zabwino pakuti pa nyengo yace tidzatuta tikapanda kufoka.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 6