Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 2:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mwa icinso Mulungu anamkwezetsa iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse,

10. kuti m'dzina la Yesu bondo liri lonse lipinde, la za m'mwamba ndi za padziko, ndi za pansi pa dziko,

11. ndi malilime onse abvomere kuti Yesu Kristu ali Ambuye, kucitira ulemu Mulungu Atate.

12. Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokha pokha pokhala ine ndiripo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani nchito yace ya cipulumutso canu ndi mantha, ndi kunthunthumira;

13. pakuti wakucita mwa inu kufuna ndi kucita komwe, cifukwa ca kukoma mtima kwace, ndiye Mulungu,

14. Citani zonse kopanda madandaulo ndi makani,

15. kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda cirema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,

16. akuonetsera mau a movo; kuti ine ndikakhale wakudzitamandira: nao m'tsiku la Kristu, kuti sindinathamanga cabe, kapena kugwiritsa nchito cabe.

17. Komatu ngatinso ndithiridwa pa nsembe ndi kutumikira kwa cikhulupiriro canu, ndikondwera, ndipo ndikondwera pamodzi ndi inu nonse;

18. momwemonso kondwerani inu, nimukondwere pamodzi ndi ine.

19. Koma ndiyembekeza mwa Ambuye Yesu kuti ndidzatumiza Timoteo kwa inu msanga, kuti inenso nditonthozeke bwino pozindikira za kwa inu.

20. Pakuti ndiribe wina wa mtima womwewo, amene adza: samalira za kwa inu ndi mtima woona.

21. Pakuti onsewa atsata za iwo okha, si za Yesu Kristu.

22. Koma muzindikira matsimikizidwe ace, kuti, monga mwana acitira atate wace, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino.

23. Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posacedwa m'mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani;

24. koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 2