Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Atesalonika 1:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PAULO, ndi Silvano, ndi Timoteo, kwa Mpingo wa Atesalonika mwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Kristu:

2. Cisomo kwa inu ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Kristu.

3. Tiziyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa ca inu, abale, monga kuyenera; pakuti cikhulupiriro canu cikula cikulire, ndipo cicurukira cikondanoca inu nonse, yense pa mnzace;

4. kotero kuti ife tokha tidzitamandira za inu m'Mipingo ya Mulungu, cifukwa ca cipiriro canu, ndi cikhulupiriro canu, m'mazunzo anu onse ndi zisautsozo muzimva;

5. ndico citsimikizo ca ciweruziro colungama ca Mulungu; kuti mu-kawerengedwe oyenera ufumu wa Mulungu, umenenso mumvera zowawa;

6. popeza nkolungama kwa Mulungu kubwezera cisautso kwa iwo akucitira inu cisautso,

7. ndi kwa inu akumva cisautso mpumulo pamodzi ndi ire, pa bvumbulutso la Ambuye Yesu wocokera Kumwamba pamodzi ndi angelo a mphamvu yace,

Werengani mutu wathunthu 2 Atesalonika 1