Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 1 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PAULO, ndi Silvano, ndi Timoteo, kwa Mpingo wa Atesalonika mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Kristu: Cisomo kwa inu ndi mtendere.

Zipatso za Uthenga Wabwino ku Tesalonika

2. Tiyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa ca inu nonse, ndi kukumbukila inu m'mapemphero athu;

3. ndi kukumbukila kosalekeza nchito yanu ya cikhulupiriro, ndi cikondi cocitacita, ndi cipiriro ca ciyembekezo ca Ambuye wathu Yesu Kristu, pamaso pa Mulungu Atate wathu;

4. podziwa, abale okondedwa ndi Mulungu, cisankhidwe canu,

5. kuti Vthenga Wabwino wathu sunadza kwa inu m'mau mokha, komatunso mumphamvu, ndi mwa Mzimu Woyera, ndi m'kucuruka kwakukuru; monga mudziwa tinakhala onga otani mwa inu cifukwa ca inu.

6. Ndipo munayamba kukhala akutsanza athu, ndi a Ambuye, m'mene mudalandira mauwo m'cisautso cambiri, ndi cimwemwe ca Mzimu Woyera;

7. kotero kuti munayamba kukhala inu citsanzo kwa onse akukhulupira m'Makedoniya ndi m'Akaya.

8. Pakuti kuturuka kwa inu kudamveka mau a Ambuye, osati m'Makedoniya ndi Akaya mokha, komatu m'malo monse cikhulupiriro canu ca kwa Mulungu cidaturuka; kotero kuti sikufunika kwa ife kulankhula kanthu.

9. Pakuti iwo okha alalikira za ife, malowedwe athu a kwa inu anali otani; ndi kuti munatembeoukira kwa Mulungu posiyana nao mafano, kutumikira Mulungu weni weni wamoyo,

10. ndi kulindirira Mwana wace acokere Kumwamba, amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu, wotipulumutsa ife ku mkwiyo ulinkudza.