Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 8:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Koma tsopano sindidzakhala kwa otsala a anthu awa monga momwe ndinakhalira masiku oyamba, ati Yehova wa makamu.

12. Pakuti padzakhala mbeu ya mtendere; mpesa udzapatsa zipatso zace, ndi nthaka idzapatsa zobala zace, ndi miyamba Idzapatsa mame ao; ndipo ndidzalandiritsa otsala a anthu awa izi zonse, cikhale colowa cao.

13. Ndipo kudzacitika kuti, monga munali cotembereretsa mwa amitundu, inu nyumba ya Yuda, ndi nyumba ya Israyeli, momwemo ndidzakusungani, ndipo mudzakhala codalitsa naco; musaope, alimbike manja anu.

14. Pakuti atero Yehova wa makamu: Monga ndil nalingirira kucitira inu coipa, muja makolo anu anautsa mkwiyo wanga, ati Yehova wa makamu, ndipo sindinawaleka;

15. momwemonso ndinalingirira masiku ano kucitira cokoma Yerusalemu ndi nyumba ya Yuda; musaopa.

16. Izi ndizo muzicite: Nenani coonadi yense ndi mnzace; weruzani zoona ndi ciweruzo ca mtendere m'zipata zanu;

17. ndipo musalingirira coipa m'mtima mwanu yense pa mnzace; nimusakonde lumbiro lonama; pakuti izi zonse ndidana nazo, ati Yehova.

18. Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,

19. Atero Yehova wa makamu: Kusala kwa mwezi wacinai, ndi kusala kwa mwezi wacisanu, ndi kusala kwa mwezi wacisanu ndi ciwiri, ndi kusala kwa mwezi wakhumi kukhale kwa nyumba ya Yuda cimwemwe ndi cikondwerero, ndi nyengo zoikika zosekerera; cifukwa cace kondani coonadi ndi mtendere.

20. Atero Yehova wa makamu: Kudzacitikanso kuti mitundu ya anthu, ndi okhalamo m'midzi yambiri adzafika,

21. ndi okhala m'mudzi umodzi adzamuka ku mudzi wina, ndi kuti, Tiyeni msanga kukapepeza Yehova, ndi kufunafuna Yehova wa makamu; ndimuka inenso.

22. Inde, mitundu yambiri ya anthu, ndi amitundu amphamvu adzadza kufunafuna Yehova wa makamu m'Yerusalemu, ndi kupepeza Yehova.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 8