Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zefaniya 3:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti pamenepo ndidzapatsa mitundu ya anthu mlomo woyera, kuti onsewa aitanire pa dzina la Yehova kumtumikira ndi mtima umodzi.

10. Kucokera tsidya lija la mitsinje ya Kusi ondipembedza, ndiwo mwana wamkazi wa obalalika anga, adzabwera naco copereka canga.

11. Tsiku ilo sudzacita manyazi ndi zocita zako zonse unandilakwira nazo; pakuti pamenepo ndidzacotsa pakati pako amene akondwera ndi kudzikuza kwako, ndipo sudzacita kudzikuzanso m'phiri langa lopatulika.

12. Koma ndidzasiya pakati pako anthu ozunzika ndi osauka, ndipo iwo adzakhulupirira dzina la Yehova.

13. Otsala a Israyeli sadzacita cosalungama, kapena kunena mabodza; ndi m'kamwa mwao simudzapezeka lilime lonyenga; pakuti adzadya nadzagona pansi, ndi palibe wakuwaopsa.

14. Yimba, mwana wamkazi wa Ziyoni; pfuula, Israyeli; kondwera nusekerere ndi mtima wonse, mwana wamkazi wa Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Zefaniya 3