Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 9:12-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mkate wathu uwu tinadzitengera kamba m'nyumba zathu, ukali wamoto, tsiku loturuka Ife kudza kwanu kuno; koma tsopano, taonani, uli wouma ndi woyaoga nkhungu;

13. ndi matumba a vinyo awa tinawadzaza akali atsopano; ndipo taonani, ang'ambika; ndi malaya athu awa ndi nsapato zathu zatha, cifukwa ca ulendo wocokera kutali ndithu.

14. Pamenepo amunawo analandirako kamba wao, osafunsira pakamwa pa Yehova.

15. Ndipo Yoswa anacitirana nao mtendere, napangana nao, akhale amoyo; ndi akalonga a msonkhano anawalumbirira,

16. Ndipo kunali, atatha kupangana nao masiku atatu, anamva kuti ndiwo anansi ao, ndi kuti kwao ndi pakati pao,

17. Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo, nafika ku midzi yap tsiku lacitatu. Koma midzi yao ndiyo Gibeoni, ndi Cefira, ndi Beerotu ndi KiriyatuYearimu.

18. Ndipo ana a Israyeli sanawakantha, pakuti akalonga a msonkhano adawalumbirira kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli. Ndipo msonkhano wonse unadandaula pa akalonga,

19. Koma akalonga onse ananena kwa msonkhano wonse, Tinawalumbirira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli, m'mwemo sitikhoza kuwacitira kanthu.

20. Tidzawacitira ici, ndi kuwasunga amoyo; ungatigwere mkwiyo cifukwa ca lumbirolo tidawalumbirira.

21. Ndipo akalonga ananena nao, Akhale ndi moyo; ndipo anasanduka akutema nkhuni, ndi otungira madzi msonkhano wonse; monga akalonga adanena nao.

22. Ndipo Yoswa anawaitana, nanena nao, kuti, Mwatinyenga cifukwa ninji, ndi kuti, Tikhala kutaritari ndi inu, pokhala kwanu kuli pakati pa ife?

23. Ndipo tsopano mukhale otembereredwa, palibe mmodzi wa inu adzamasuka wosakhala kapolo, ndi kutemera nkhuni, ndi kutungira madzi nyumba ya Mulungu wanga.

24. Ndipo anamyankha Yoswa nati, Popeza anatiuzitsa akapolo anu kuti Yehova Mulungu wanu analamulira mtumiki wace Mose kukupatsani dziko lonseli, ndi kupasula nzika zonse za m'dziko pamaso panu; potero tinaopera kwambiri moyo wathu pamaso panu, ndipo tinacita cinthuci.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 9