25. Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.
26. Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.
27. Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.
28. Ndipo Yoswa anatentha Ai, nausandutsa muunda ku nthawi yonse, bwinja kufikira lero lino.