Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 7:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo Akani anayankha Yoswa nati, Zoonadi, ndacimwira Yehova Mulungu wa Israyeli, ndacita zakuti zakuti;

21. pamene ndinaona pazofunkha maraya abwino a ku Babulo, ndi masekeli mazana awiri a siliva, ndi cikute cagolidi, kulemera kwace masekeli makumi asanu, ndinazikhumbira ndi kuzitenga; ndipo taonani, ndazibisa m'nthaka pakati pa hema wanga, ndi siliva pansi pacepo.

22. Pamenepo Yoswa anatuma mithenga, iwo nathamangira kuhema; ndipo taonani, zidabisika m'hema mwace ndi siliva pansi pace.

23. Ndipo anazicotsa pakati pa hema, nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa ana onse a Israyeli, nazitula pamaso pa Yehova.

24. Ndipo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anatenga Akani mwana wa Zera, ndi siliva, ndi marayawo, ndi cikute cagolidi, ndi ana ace amuna ndi akazi, ndi ng'ombe zace, ndi aburu ace, ndi nkhosa zace, ndi hema wace ndi zace zonse; nakwera nazo ku cigwa ca Akori.

25. Ndipo Yoswa anati, Watisautsiranji? Yehova adzakusautsa lero lino. Ndipo, Aisrayeli onse anamponya miyala, nawatentha ndi moto, nawaponya miyala.

26. Ndipo anamuuniikira mulu waukuru wamiyala, wokhalako kufikira lero lino; ndipo Yehova anatembenuka kusiya mkwiyo wace waukuru. Cifukwa cace anacha dzina lace la malowo, Cigwa ca Akori, mpaka lero lino.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 7