Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 7:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo Yoswa anati kwa Akani, Mwana wanga, ucitiretu ulemu Yehova Mulungu wa Israyeli, numlemekeze iye; nundiuze tsopano, wacitanji? usandibisire.

20. Ndipo Akani anayankha Yoswa nati, Zoonadi, ndacimwira Yehova Mulungu wa Israyeli, ndacita zakuti zakuti;

21. pamene ndinaona pazofunkha maraya abwino a ku Babulo, ndi masekeli mazana awiri a siliva, ndi cikute cagolidi, kulemera kwace masekeli makumi asanu, ndinazikhumbira ndi kuzitenga; ndipo taonani, ndazibisa m'nthaka pakati pa hema wanga, ndi siliva pansi pacepo.

22. Pamenepo Yoswa anatuma mithenga, iwo nathamangira kuhema; ndipo taonani, zidabisika m'hema mwace ndi siliva pansi pace.

23. Ndipo anazicotsa pakati pa hema, nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa ana onse a Israyeli, nazitula pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 7