Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 6:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Nati kwa anthu, Pitani, muzizungulira mudzi, ndi ankhondo ndi zida zao atsogolere likasa la Yehova.

8. Ndipo atanena kwa anthu Yoswa, ansembe asanu ndi awiri akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo pamaso pa Yehova, anapita naliza mphalasazo; ndipo likasa la cipangano ca Yehova linawatsata.

9. Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m'mbuyo anatsata likasa, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

10. Ndipo Yoswa analamulira anthu, ndi kuti, Musamapfuula, kapena kumveketsa mau anu, asaturuke konse mau m'kamwa mwanu, mpaka tsiku lakunena nanu ine, Pfuulani; pamenepo muzipfuula.

11. Ndipo anazungulitsa likasa la Yehova mudzi, kuzungulira kamodzi; pamenepo analowa kucigono, nagona m'mwemo.

12. Ndipo Yoswa analawira mamawa, ndi ansembe anasenza likasa la Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 6