Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 6:25-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma Rahabi, mkazi wadamayo ndi banja la atate wace, ndi onse anali nao, Yoswa anawasunga ndi moyo; ndipo anakhala pakati pa Israyeli mpaka lero tino; cifukwa anabisa mithenga imene Yoswa anaituma kuzonda Yeriko.

26. Ndipo Yoswa anawalumbirira nyengo ija, ndi kuti, Wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzauka ndi kumanga mudzi uwu wa Yeriko; adzamanga kuzika kwace ndi kutayapo mwana wace woyamba, nadzaimika zitseko zace ndi kutayapo mwana wace wotsirizira.

27. Potero Yehova anakhala ndi Yoswa; ndi mbiri yace inabuka m'dziko lonse.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 6