Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 22:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Pamene ana a Israyeli anamva ici msonkhano wonse wa ana a Israyeli anasonkhana ku Silo, kuti awakwerere kuwathira nkhondo.

13. Ndipo ana a Israyeli anatumiza kwa ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ku dziko la Gileadi, Pinehasi mwana wa Eleazare wansembe,

14. ndi akalonga khumi naye; nyumba imodzi ya atate kalonga mmodzi, kotero ndi mapfuko onse a Israyeli; yense wa iwowa ndiye mkuru wa nyumba ya atate ao mwa mabanja a Israyeli.

15. M'mene anafika kwa ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ku dziko la Gileadi, ananena nao ndi kuti,

16. Utero msonkhano wonse wa Yehova, Colakwa ici nciani mwalakwira naco Mulungu wa Israyeli, ndi kumtembenukira Yehova lero line kusamtsatanso, popeza munadzimangira guwa la nsembe kupikisana ndi Yehova lero lino?

Werengani mutu wathunthu Yoswa 22