Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 21:18-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Anatotu ndi mabusa ace, ndi Alimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

19. Miclzi yonse ya ana a Aroni, ansembe, ndiyo khumi ndi itatu, ndi mabusa ao.

20. Ndipo mabanja a ana a Kohati, Aleviwo, otsala a ana a Kohati, analandira midzi ya maere ao motapira pa pfuko la Efraimu.

21. Ndipo anawapatsa Sekemu ndi mabusa ace ku mapiri a Efraimu, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Gezeri ndi mabusa ace;

22. ndi Kibizaimu ndi mabusa ace, Betihoroni ndi mabusa ace; midzi inai.

23. Ndipo motapira m'pfuko La Dani, Eliteke ndi mabusa ace, Gibetoni ndi mabusa ace;

24. Aijaloni ndi mabusa ace, Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

25. Ndipo motapira pa pfukola Manaselogawika pakati, Taanaki ndi mabusa ace, ndi Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi iwiri.

26. Midzi yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.

27. Ndipo anapatsa ana a Gerisoni, a mabanja a Alevi, motapira pa pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo; ndi Beesitera ndi mabusa ace; midzi iwiri.

28. Ndipo motapira pa pfuko la Isakara, Kisioni ndi mabusa ace, Daberati ndi mabusa ace;

29. Yarimutu ndi mabusa ace, Eniganimu ndi mabusa ace; midzi inai.

30. Ndipo motapira pa pfuko La Aseri, Misali ndi mabusa ace, Abidoni ndi mabusa ace;

31. Helikati ndi mabusa ace, ndi Rehobo ndi mabusa ace; midzi inai.

32. Ndipo motapira pa pfuko la Nafitali, Kedesi m'Galileya ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Hamotidori ndi mabusa ace, ndi Karitani ndi mabusa ace, midzi itatu.

33. Midzi yonse ya Agerisoni monga mwa mabanja ao ndiyo midzi khumi ndi itatu ndi mabusa ao.

34. Ndipo anapatsa kwa mabanja a ana a Merari, otsala a Alevi, motapira pa pfuko la Zebuloni, Yokineamu ndi mabusa ace, ndi Karita ndi mabusa ace,

35. Dimna ndi mabusa ace, Nahalala ndi mabusa ace; midzi inai.

36. Ndipo motapira pa pfuko la Rubeni, Bezeri ndi mabusa ace, ndi Yahazi ndi mabusa ace,

Werengani mutu wathunthu Yoswa 21